Deuteronomo 9:22-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ku Tabera, ndi ku Masa, ndi ku Kibiroti Hatava, munautsanso mkwiyo wa Yehova.

23. Ndipo pamene Yehova anakutumizani kucokera ku Kadesi Barinea, ndi kuti, Kwerani, landirani dziko limene ndakupatsani; munapikisana nao mau a Yehova Mulungu wanu, osamkhulupirira, kapena kumvera mau ace.

24. Munakhala opikisana ndi Yehova kuyambira tsikuli ndinakudziwani.

25. Ndipo ndinagwa pansi pamaso pa Yehova masiku makumi anai usana ndi usiku ndinagwa pansiwa; popeza Yehova adati kuti adzakuonongani.

Deuteronomo 9