38. kupitikitsa amitundu akuru ndi amphamvu oposa inu pamaso panu, kukulowetsani ndi kukupatsani dziko lao likhale colowa canu, monga lero lino.
39. Potero dziwani lero tino nimukumbukire m'mtima mwanu, kuti Yehova ndiye Mulungu, m'thambo la kumwamba ndi pa dziko lapansi; palibe wina.
40. Muzisunga malemba ace, ndi malamulo ace, amene ndikuzuzani lero lino, kuti cikukomereni inu ndi ana anu akukutsatani, ndi kuti masiku anu acuruke pa dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanu kosatha.
41. Pamenepo Mose anapatula midzi itatu tsidya lija la Yordano loturuka dzuwa;