Deuteronomo 33:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo mdalitso, Mose munthu wa Mulungu anadalitsa nao ana a Israyeli asanafe, ndi uwu.

2. Ndipo anati,Yehova anafuma ku Sinai,Nawaturukiraku Seiri;Anaoneka wowala pa phiri la Parana,Anafumira kwa opatulika zikwi zikwi;Ku dzanja lamanja lace kudawakhalira lamulo lamoto.

3. Inde akonda mitundu ya anthu;Opatulidwa ace onse ali m'dzanjamwanu;Ndipo akhala pansi ku mapazi anu;Yense adzalandirako mau anu.

4. Mose anatiuza cilamulo,Colowa ca msonkhano wa Yakobo.

5. Ndipo iye anali mfumu m'Yesuruni,Pakusonkhana mafumu a anthu,Pamodzi ndi mapfuko a Israyeli.

6. Rubeni akhale ndi moyo, asafe,Koma amuna ace akhale owerengeka.

7. Za Yuda ndi izi; ndipo anati,Imvani, Yehova, mau a Yuda,Ndipo mumfikitse kwa anthu ace;Manja ace amfikire;Ndipo mukhale inu thandizo lace pa iwo akumuukira.

Deuteronomo 33