Deuteronomo 32:22-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Pakuti wayaka moto mu mkwiyo wanga,Utentha kumanda kunsiUkutha dziko lapansi ndi zipatso zaceNuyatsa maziko a mapiri,

23. Ndidzawaunjikira zoipa;Ndidzawathera nubvi yanga.

24. Adzaonda nayo njalaAdzanyekeka ndi makala a moto, cionongeko cowawa;Ndipo ndidzawatumizira mana a zirombo,Ndi ululu wa zokwawa m'pfumbi.

25. Pabwalo lupanga lidzalanda,Ndi m'zipinda mantha;Lidzaononga mnyamata ndi namwali,Woyamwa pamodzi ndi munthu waimvi.

26. Ndinati, Ndikadawauzira ndithu,Ndikadafafaniza cikumbukiro cao mwa anthu;

Deuteronomo 32