19. Ndicititsa mboni lero kumwamba ndi dziko lapansi zitsutse inu; ndaika pamaso panu moyo ndi imfa, mdalitso ndi temberero; potero, sankhani moyo, kuti mukhale ndi moyo, inu ndi mbeu zanu;
20. kukonda Yehova Mulungu wanu, kumvera mau ace, ndi kummamatira iye, tr pakuti iye ndiye moyo wanu, ndi masiku anu ocuruka; kuti mukhale m'dziko limene Yehova analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isake, ndi Yakobo, kuwapatsa ili.