14. Koma sindicita cipangano ici ndi lumbiro ili ndi inu nokha;
15. komanso ndi iye wakuimirira pano nafe lero lino pamaso pa Yehova Mulungu wathu, ndiponso ndi iye wosakhala pano nafe lero lino.
16. Pakuti mudziwa cikhalidwe cathu m'dziko la Aigupto, ndi kuti tinapyola pakati pa amitundu amene munawapyola;
17. ndipo munapenya zonyansa zao, ndi mafano ao, mtengo ndi mwala, siliva ndi golidi, zokhala pakati pao;