Deuteronomo 28:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Zidzakhala zodala mtanga wanu, ndi coumbiramo mkate wanu.

6. Mudzakhala odala polowa inu, mudzakhala odala poturuka inu.

7. Yehova adzakantha adani anu akukuukirani; adzakudzerani njira imodzi, koma adzathawa pamaso panu njira zisanu ndi ziwiri.

8. Yehova adzakulamulirani dalitso m'nkhokwe zanu, ndi m'zonse muturutsirako dzanja lanu; ndipo adzakudalitsani m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani,

9. Yehova adzakukhazikirani yekha mtundu wa anthu wopatulika, monga anakulumbirirani; ngati mudzasunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, ndi kuyenda m'njira zace.

Deuteronomo 28