7. Ndipo muiphike ndi kuidya m'malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha; koma m'mawa mwace mubwerere kumka ku mahema anu.
8. Masiku asanu ndi limodzi muzidya mkate wopanda cotupitsa; ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri ndilo loletsa, la Yehova Mulungu wanu; musamagwira nchito pamenepo.
9. Mudziwerengere masabata asanu ndi awiri; muyambe kuwerenga masabata asanu ndi awiri poyambira kuceka tirigu waciriri.