5. Simuyenera kuphera nsembe ya Paskha m'midzi yanu iri yonse, imene Yehova Mulungu wanu akupatsani;
6. koma pamalo pamene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsapo dzina lace, pamenepo muphere nsembe ya Paskha, madzulo, polowa dzuwa, nyengo ya kuturuka inu m'Aigupto.
7. Ndipo muiphike ndi kuidya m'malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha; koma m'mawa mwace mubwerere kumka ku mahema anu.