Deuteronomo 14:11-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Mbalame zosadetsazonse muyenera kumadya.

12. Koma izi ndi zimene simuyenera kumadya: mphungu, ndi nkhwazi, ndi cikambi,

13. ndi kamtema, ndi mphamba, ndi muimba monga mwa mtundu wace;

14. ndi khungubwe ali yense monga mwa mtundu wace;

15. ndi nthiwatiwa, ndi cipudo, ndi kakoa, ndi kabawi monga mwa mtundu wace;

16. ndi nkhutukutu, ndi mancici, ndi tsekwe;

17. ndi bvuwo, ndi dembu, ndi nswankhono;

18. ndi iodwa, ndi cimeza, monga mwa mtundu wace, ndi sadzu, ndi mleme.

19. Ndipo zokwawa zonse zakuuluka muziyesa zonyansa; musamazidya.

20. Mbalame zonse zosadetsa muyenera kumadya.

Deuteronomo 14