Deuteronomo 13:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Akauka pakati pa inu mneneri, kapena wakulota maloto, nakakupatsani cizindikilo kapena cozizwa;

2. ndipo cizindikilo kapena cozizwa adanenaci cifika, ndi kuti, Titsate milungu yina, imene simunaidziwa, ndi kuitumikira;

3. musamamvera mau a mneneri uyu, kapena wolota maloto uyu; popeza Yehova Mulungu wanu akuyesani, kuti adziwe ngati mukonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse.

Deuteronomo 13