1. Akauka pakati pa inu mneneri, kapena wakulota maloto, nakakupatsani cizindikilo kapena cozizwa;
2. ndipo cizindikilo kapena cozizwa adanenaci cifika, ndi kuti, Titsate milungu yina, imene simunaidziwa, ndi kuitumikira;
3. musamamvera mau a mneneri uyu, kapena wolota maloto uyu; popeza Yehova Mulungu wanu akuyesani, kuti adziwe ngati mukonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse.