4. Musamatero ndi Yehova Mulungu wanu.
5. Koma ku malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha mwa mapfuko anu onse kuikapo dzina lace, ndiko ku cokhalamo cace, muzifunako, ndi kufikako;
6. ndi kubwera nazo kumeneko nsembe zanu zopsereza, ndi nsembe zanu zophera, ndi magawo anu onse a magawo khumi, ndi nsembe yokweza ya dzanja lanu, ndi zowinda zanu, ndi nsembe zanu zaufulu, ndi zoyamba kubadwa za ng'ombe zanu, ndi za nkhosa ndi mbuzi zanu;
7. ndipo kumeneko muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, ndi kukondwera nazo zonse mudazigwira ndi dzanja lanu, inu ndi a pa banja lanu, m'mene Yehova Mulungu wanu anakudalitsani.
8. Musamadzacita monga mwa zonse tizicita kuno lero, yense kucita ciri conse ciyenera m'maso mwace;
9. pakuti mpaka lero simunafikira mpumulo ndi colowa, zimene Yehova Mulungu wanu adzakupatsani.