Danieli 5:23-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. koma munadzikweza kutsutsana naye Ambuye wa Kumwamba; ndipo anabwera nazo zotengera za nyumba yace kwa inu; ndi inu ndi akuru anu, akazi anu ndi akazi anu ang'ono, mwamweramo vinyo; mwalemekezanso milungu yasiliva, ndi yagolidi, yamkuwa, yacitsulo, yamtengo, ndi yamwala, imene siiona, kapena kumva, kapena kudziwa; ndi Mulungu amene m'dzanja mwace muli mpweya wanu, ndi njira zanu zonse, yemweyo simunamcitira ulemu.

24. Pamenepo nsonga ya dzanja inatumidwa kucokera pamaso pace, nililembedwa lembali.

25. Ndipolembalolembedwa ndi ili: MENE MENE TEKEL UF ARSIN.

26. Kumasulira kwace kwa mau awa ndi uku: MENE, Mulungu anawerenga ufumu wanu, nautha.

27. TEKEL, Mwayesedwa pamiyeso, nimupezeka mwaperewera.

28. PERES, ufumu wanu wagawika, nuperekedwa kwa Amedi ndi Aperisi.

Danieli 5