8. Koma potsiriza pace analowa pamaso panga Danieli, dzina lace ndiye Belitsazara, monga mwa dzina la mulungu wanga, amenenso muli mzimu wa milungu yoyera m'mtima mwace; ndipo ndinamfotokozera lotoli pamaso pace, ndi kuti,
9. Belitsazara iwe, mkuru wa alembi, popeza ndidziwa kuti mwa iwe muli mzimu wa milungu yoyera, ndi kuti palibe cinsinsi cikusautsa, undifotokozere masomphenya a loto langa ndalotali, ndi kumasulira kwace.
10. Masomphenya a m'mtima mwanga pakama panga ndi awa: Ndinapenya ndi kuona mtengo pakati pa dziko lapansi, msinkhu wace ndi waukuru.
11. Mtengowo unakula, nulimba, ndi msinkhu wace unafikira kumwamba, nuonekera mpaka cilekezero ca dziko lonse lapansi.