Danieli 2:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Pamenepo cinsinsico cinabvumbulutsidwa kwa Danieli m'masomphenya a usiku. Ndipo Danieli analemekeza Mulungu wa Kumwamba.

20. Danieli anayankha, nati, Lilemekezedwe dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi, a pakuti nzeru ndi mphamvu ziri zace;

21. pakuti amasanduliza nthawi ndi nyengo, acotsa mafumu, nalonga mafumu, apatsa anzeru nzeru, ndi cidziwitso kwa iwo okhoza kuzindikira.

22. Iye abvumbulutsa zinthu zakuya ndi zinsinsi; adziwa zokhala mumdima, ndi kuunika kumakhala kwa Iye.

23. Ndikuyamikani ndi kukulemekezani Inu, Mulungu wa makolo anga, pakuti mwandipatsa nzeru ndi mphamvu; ndipo mwandidziwitsa tsopano ici tacifuna kwa Inu; pakuti mwatidziwitsa mlandu wa mfumu.

Danieli 2