Danieli 1:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo mfumu inauza Asipenazi mkuru wa adindo kuti abwere nao ena a ana a Israyeli, a mbeu ya mafumu, ndi ya akalonga;

4. anyamata opanda cirema, a maonekedwe okoma, a luso la nzeru zonse, ocenjera m'kudziwa, a luntha lakuganizira, okhoza kuimirira m'cinyumba ca mfumu; ndi kuti awaphunzitse m'mabuku, ndi manenedwe a Akasidi.

5. Ndipo mfumu inawaikira gawo la cakudya ca mfumu tsiku ndi tsiku, ndi la vinyo wakumwa iye, ndi kuti awalere zaka zitatu, kuti potsiriza pace aimirire pamaso pa mfumu.

6. Mwa awa tsono munali a ana a Yuda, Danieli, Hananiya, Misayeli, ndi Azariya.

7. Ndi mkuru wa adindo anawapatsa maina ena; Danieli anamucha Belitsazara; ndi Hananiya, Sadrake; ndi Misaeli, Mesaki; ndi Azariya, Abedinego.

Danieli 1