Cibvumbulutso 4:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo mu mpando wacifumu mudaturuka mphezi ndi mau ndi mabingu. Ndipo panali nyali zisanu ndi ziwiri za mota zoyaka ku mpando wacifumu, ndiyo Mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu;

6. ndipo ku mpandowo, ngati nyanja, yamandala yonga krustalo; ndipopakati pa mpandowo, ndi pozinga mpandowo, zamoyo zinai zodzaia ndi maso kutsogolo indi kumbuyo.

7. Ndipo camoyo coyamba cinafanana nao mkango, ndi camoyo caciwiri cinafanana ndi mwana wa ng'ombe, ndi camoyo cacitatu cinali nayo nkhope yace ngati ya munthu, ndi camoyo cacinai cidafanana ndi ciombankhanga cakuuluka.

8. Ndipo zamoyozo zinai, conse pa cokha cinali nao mapiko asanu ndi limodzi; ndipo zinadzala ndi maso pozinga ponse ndi m'katimo; ndipo sizipumula usana ndi usiku, ndi kunena, Woyera, woyera, woyera, Ambuye Mulungu Wamphamvuyonse, amene anali, amene ali, ndi amene alinkudza.

Cibvumbulutso 4