Cibvumbulutso 22:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo Mzimu ndi mkwatibwi anena, Idzani, Ndipo wakumva anene, Idzani. Ndipo wakumva ludzu adze; iye wofuna, atenge madzi a moyo kwaulere.

18. Ndicita umboni kwa munthu ali yense wakumva mau a cinenero ca buku ili, 1 Munthu akaonjeza pa awa, adzamuonjezera Mulungu miliri yolembedwa m'bukumu:

19. ndipo 2 ali yense akacotsako pa mau a buku la cinenero ici, Mulungu adzamcotsera gawo lace pa mtengo wa moyo, ndi 3 m'mzinda woyerawo, ndi pa izi zilembedwa m'bukumu.

20. Iye wakucitira umboni izi, anena, 4 Indetu; ndidza msanga. Amen; idzani, Ambuye Yesu.

Cibvumbulutso 22