12. Ndipo maso ace ali lawi la moto, ndi pamutu pace pali nduwira zacifumu zambiri; ndipo ali nalo dzina lolembedwa, wosalidziwa wina yense koma iye yekha.
13. Ndipo abvala cobvala cowazidwa mwazi; ndipo achedwa dzina lace, Mau a Mulungu.
14. Ndipo magulu a nkhondo okhala m'Mwamba anamtsata iye, okwera pa akavalo oyera, obvala bafuta woyera woti mbu.