Aroma 9:29-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Ndipo monga Yesaya anati kale,4 Ngati Ambuye wa makamu a kumwamba sanatisiyira ife mbeu,Tikadakhala monga Sodoma, ndipo tikadafanana ndi Gomora.

30. Cifukwa cace tidzatani? 5 Kuti amitundu amene sanatsata cilungamo, anafikira cilungamo, ndico cilungamo ca cikhulupiriro;

31. 6 koma Israyeli, potsata lamulo la cilungamo, sanafikira lamulolo.

32. Cifukwa canji? Cifukwa kuti sanacitsata ndi cikhulupiriro, koma monga ngati ndi nchito. 7 Anakhumudwa pa mwala wokhumudwitsa;

Aroma 9