Aroma 9:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. 1 Ndipo kudzali, kuti pamalo pamenepo kunanenedwa kwa iwo, Simuli anthu anga ai,Pomwepo iwo adzachedwa ana a Mulungu wamoyo.

27. Ndipo Yesaya apfuula za Israyeli, kuti,2 Ungakhale unyinji wa ana a Israyeli ukhala monga mcenga wa kunyanja, 3 cotsalira ndico cidzapulumuka.

28. Pakuti Ambuye adzacita mau ace pa dziko lapansi, kuwatsiriza mwacidule.

29. Ndipo monga Yesaya anati kale,4 Ngati Ambuye wa makamu a kumwamba sanatisiyira ife mbeu,Tikadakhala monga Sodoma, ndipo tikadafanana ndi Gomora.

Aroma 9