Aroma 9:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndinena zoona mwa Kristu, sindinama ai, cikumbu mtima canga cicita umboni pamodzi ndine mwa Mzimu Woyera,

2. kuti ndagwidwa ndi cisoni cacikuru ndi kuphwetekwa mtima kosaleka.

3. Pakuti ndikadafunakuti ine ndekha nditembereredwe kundicotsa kwa Kristu cifukwa ca abale anga, ndiwo a mtundu wanga monga mwa thupi;

4. ndiwo Aisrayeli; ali nao umwana, ndi ulemerero, ndi mapangano, ndi kupatsa kwa malamulo, ndi kutumikira m'kacisi wa Mulungu, ndi malonjezo;

Aroma 9