Aroma 7:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo cotero odipeza lamulo ili, kuti, pamene ndifuna cabwino, coipa ciriko.

22. Pakuti monga mwa munthu wa m'kati mwanga, ine ndikondwera ndi cilamulo ca Mulungu:

23. koma ndiona lamulo lina m'ziwalo zanga, lirikulimbana ndi lamulo la mtima wanga, ndi kundigonjetsa kapolo wa lamulo la m'ziwalo zanga.

24. Munthu wosauka ine; adzandilanditsa ndani m'thupi la imfa iyi?

Aroma 7