1. Cifukwa cace tidzatani? Tidzakhalabe m'ucimo kodi, kuti cisomo cicuruke?
2. Msatero ai. Ife amene tiri akufa ku ucimo, tidzakhala bwanji cikhalire m'menemo?
3. Kapena kodi simudziwa kuti ife tonse amene tinabatizidwa mwa Kristu Yesu; tinabatizidwa mu imfa yace?