18. Cifukwa cace, monga mwa kulakwa kumodzi kutsutsa kunafikira anthu onse; comweconso mwa cilungamitso cimodzi cilungamo ca moyo cinafikira anthu onse.
19. Pakuti monga ndi kusamvera kwa munthu mmodzi ambiri anayesedwa ocimwa, comweco ndi kumvera kwa mmodzi ambiri adzayesedwa olungama.
20. Ndipo lamulo linalowa moyenjezera, kuti kulakwa kukacuruke; koma rl pamene ucimo unacuruka, pomwepo cisomo cinacuruka koposa;
21. kuti, mongaucimo unacita ufumu muimfa, comweconso cisomo cikacite ufumu mwa cilungamo, kufikira moyo wosatha mwa Yesu Kristu Ambuye wathu.