9. Cikondano cikhale copanda cinyengo, Dana naco coipa; gwirizana naco cabwino.
10. M'cikondano ca anzanu wina ndi mnzace mukondane ndi cikondi ceni ceni; mutsogolerane ndi kucitira wina mnzace ulemu;
11. musakhale aulesi m'macitidwe anu; khalani acangu mumzimu, tumikirani Ambuye;
12. kondwerani m'ciyembekezo, pirirani m'masautso; limbikani cilimbikire m'kupemphera,
13. Patsani zosowa oyera mtima; cerezani aulendo.
14. Dalitsani iwo akuzunza inu; dalitsani, musawatemberere.