Aroma 12:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. kondwerani m'ciyembekezo, pirirani m'masautso; limbikani cilimbikire m'kupemphera,

13. Patsani zosowa oyera mtima; cerezani aulendo.

14. Dalitsani iwo akuzunza inu; dalitsani, musawatemberere.

15. Kondwani nao iwo akukondwera; lirani nao akulira.

16. Mukhale ndi mtima umodzi wina ndi mnzace. Musasamalire zinthu zazikuru, koma phatikanani nao odzicepetsa, Musadziyesere anzeru mwa inu nokha.

17. Musabwezere munthu ali yense coipa cosinthana ndi coipa. Ganiziranitu zinthu za ulemu pamaso pa anthu onse.

Aroma 12