Amosi 6:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Pitani ku Kaline, nimuone; kucokera komweko mupite ku Hamati wamkulu mutsikire ku Gati wa Afilisti; kodi awo ndi okoma koposa maufumu ano? kapena malire ao aposa malire anu?

3. Inu akutalikitsa tsiku loipa, ndi kusendeza pafupi mpando waciwawa;

4. ogona pa makama aminyanga, nadzithinula pa maguwa ao ogonapo, nadya ana a nkhosa a ku zoweta, ndi ana a ng'ombe ocoka pakati pa khola;

5. akungoyimba kutsata maliridwe a zeze, nadzilingiririra zoyimbira nazo Ingati Davide;

6. akumwera vinyo m'zipanda, nadzidzoza ndi mafuta abwino oposa, osagwidwa cisoni ndi kutyoka kwa Yosefe.

7. Cifukwa cace tsono, adzatengedwa ndende ndi oyamba kutengedwa ndende; ndi phokoso la iwo odzithinula lidzapita.

Amosi 6