Amosi 5:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. koma musamafuna Beteli, kapena kumalowa m'Giligala; musamapita ku Beereseba; pakuti Giligala adzalowadi m'ndende, ndi Beteli adzasanduka cabe.

6. Funani Yehova, ndipo mudzakhala ndi mayo; angabuke ngati moto m'nyumba ya Yosefe, ndipo unganyeke wopanda wakuzima m'Beteli;

7. inu osintha ciweruzo cikhale civumulo, nimugwetsa pansi cilungamo,

8. Iye wakulenga Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, nasanduliza mdima wandiweyani ukhale m'mawa, nasanduliza usana ude ngati usiku, wakuitana madzi a m'nyanja, nawatsanulira pa dziko lapansi, dzina lace ndiye Yehova;

9. wakufikitsa cionongeko pa wamphamvu modzidzimuka, cionongeko nicigwera linga,

10. Iwo adana naye wodzudzula kucipata, nanyansidwa naye wolunjikitsa mau.

Amosi 5