Amosi 2:14-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo populumukirapo padzasowera waliwiro, ndi wamphamvu; sadzalimbikitsa mphamvu yace, ndi ngwazi siidzapulumutsa moyo wace;

15. ndi wokoka uta sadzalimbika, ndi waliwiro sadzadzipulumutsa; ngakhale woyenda pa akavalo sadzapulumutsa moyo wace;

16. ndi wolimba mtima mwa ngwazi adzathawa wamarisece tsiku lomwelo, ati Yehova.

Amosi 2