Amosi 1:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. koma ndidzatumiza moto pa linga la Turo, ndipo udzanyeketsa nyumba zace zacifumu.

11. Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Edomu, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza analondola mphwace ndi lupanga, nafetsa cifundo cace conse, ndi mkwiyo wace unang'amba cing'ambire, nasunga mkwiyo wace cisungire;

12. koma ndidzatumiza moto pa Temani, udzanyeketsa nyumba zacifumu za Bozira.

13. Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za ana a Amoni, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anatumbula akazi ali m'pakati a Gileadi, kuti akuze malire ao;

14. koma ndidzayatsa moto pa linga la Raba, udzanyeketsa nyumba zacifumu zace, ndi kupfuula tsiku la nkhondo, ndi namondwe, tsiku la kabvumvulu;

15. ndipo mfumu yao idzalowa kundende, iyo ndi akalonga ace pamodzi, ati Yehova.

Amosi 1