Akolose 3:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Cifukwa cace fetsani ziwalozo ziri padziko; dama, cidetso, cifunitso ca manyazi, cilakolako coipa, nelicisiriro, cimene ciri kupembedza mafano;

6. cifukwa ca izi zomwe ukudza mkwiyo wa Mulungu pa ana a kusamvera;

7. zimene munayendamo inunso kale, pamene munakhala ndi moyo wanu m'menemo,

8. Koma tsopano tayani inunso zonsezi: mkwiyo, kupsa mtima, dumbo, mwano, zonyansa zoturuka m'kamwa mwanu:

9. musamanamizana wina ndi mnzace; popeza mudabvula munthu wakale pamodzi ndi nchito zace,

10. ndipo munabvala watsopano, amene alikukonzekawatsopano, kuti akhale naco cizindikiritso, mousa mwa cifaniziro ca iye amene anamlenga iye;

Akolose 3