Akolose 3:2-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Lingalirani zakumwamba osati za padziko ai.

3. Pakuti munafa, ndipo moyo wanu wabisika pamodzi ndi Kristu mwa Mulungu,

4. Pamene Kristu adzaoneka, ndiye moyo wathu, pamenepo inunso mudzaonekera pamodzi ndi iye m'ulemerero.

5. Cifukwa cace fetsani ziwalozo ziri padziko; dama, cidetso, cifunitso ca manyazi, cilakolako coipa, nelicisiriro, cimene ciri kupembedza mafano;

6. cifukwa ca izi zomwe ukudza mkwiyo wa Mulungu pa ana a kusamvera;

7. zimene munayendamo inunso kale, pamene munakhala ndi moyo wanu m'menemo,

8. Koma tsopano tayani inunso zonsezi: mkwiyo, kupsa mtima, dumbo, mwano, zonyansa zoturuka m'kamwa mwanu:

Akolose 3