27. Ndi cikhulupiriro anasiya Aigupto, wosaopa mkwiyo wa mfumu; pakuti anapirira molimbika monga ngari kuona wosaonekayo.
28. Ndi cikhulupiriro 1 anacita Paskha, ndi kuwaza kwa mwazi, kuti wakuononga ana oyamba angawakhudze iwo.
29. Ndi cikhulupiriro 2 anaoloka Nyanja Yofiira kupita ngati pamtunda: ndiko Aaigupto poyesanso anamizidwa.
30. Ndi cikhulupiriro 3 malinga a Yeriko adagwa atazunguliridwa masiku asanu ndi awiri.