Ahebri 11:15-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipotu akadakumbukila lijalo adaturukamo akadaona njira yakubwera nayo.

16. Koma tsopano akhumba lina loposa, ndilo la m'Mwamba; mwa ici Mulungu sacita manyazi nao poitanidwa Mulungu wao; pakuti adawakonzera mudzi.

17. Ndi cikhulupiriro Abrahamu, poyesedwa, anapereka nsembe Isake, ndipo iye amene adalandira malonjezano anapereka mwana wace wayekha;

18. amene kudanenedwa za iye, kuti, Mwa Isake mbeu yako idzaitanidwa:

19. poyesera iye kuti Mulungu ngwokhoza kuukitsa, ngakhale kwa akufa; kucokera komwe, paciphiphiritso, anamlandiranso.

20. Ndi cikhulupiriro Isake anadalitsa Yakobo ndi Esau, zingakhale za zinthu zirinkudza,

Ahebri 11