3. Komatu mu izizo muli cikumbukiro ca macimo caka ndi caka.
4. Pakuti sikutheka kuti mwazi wa ng'ombe zamphongo, ndimbuzi ukacotsera macimo.
5. Mwa ici polowa m'dziko lapansi, anena,Nsembe ndi copereka simunazifuna,Koma thupi munandikonzera Ine.
6. Nsembe zopsereza zamphumphu ndi za kwa macimo simunakondwera nazo;
7. Pamenepo ndinati, Taonani, ndafika,(Pamutu pace pa buku palembedwa za Ine)Kudzacita cifuniro canu, Mulungu,