Ahebri 10:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndi cifuniro cimeneco tayeretsedwa mwa copereka ca thupi la Yesu Kristu, kamodzi, kwatha.

11. Ndipotu wansembe ali yenseamaima tsiku ndi tsiku, natumikira, napereka nsembe zomwezi kawiri kawiri, zimene sizikhoza konse kucotsa macimo;

12. koma iye, m'mene adapereka nsembe imodzi cifukwa ca macimo, anakhala pa dzanja lamanja la Mulungu cikhalire;

13. kuyambira pomwepo alindirira, kufikira adani ace aikidwa akhale mpando ku mapazi ace.

14. Pakuti ndi cipereko cimodzi anawayesera angwiro cikhalire iwo oyeretsedwa.

15. Koma Mzimu Woyeranso aticitira umboni; pakuti adatha kunena,

Ahebri 10