1. Abale, ngatinso munthu agwidwa nako kulakwa kwakuti, inu auzimu, mubweze wotereyo mu mzimu wa cifatso; ndikudzipenyerera wekha, ungayesedwe nawenso.
2. Nyamuliranani zothodwetsa, ndipo kotero mufitse cilamulo ca Kristu.
3. Pakuti ngati wina ayesa ali kanthu pokhala ali cabe, adzinyenga yekha.