Agalatiya 5:3-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndicitanso umboni kwa munthu yense wolola amdule, kuti ali wamangawa kucita cilamulo conse.

4. Mulibe kanthu ndi Kristu, inu amene muyesedwa olungama ndi lamulo; mudagwa posiyana naco cisomo.

5. Pakuti ife mwa Mzimu, kucokera m'cikhulupiriro, tilindira ciyembekezo ca cilungamo,

6. Pakuti mwa Kristu Yesu kapena mdulidwe kapena kusadulidwa kulibe mphamvu; komatu cikhulupiriro cakucititsa mwa cikondi.

7. Munathamanga bwino; anakuletsani ndani kuti musamvere coonadi?

8. Kukopa kumene sikucokera kwa iye anakuitanani.

9. Cotupitsa pang'ono citupitsa mtanda wonse.

10. Ine ndikhulupirira inu mwa Ambuye, kuti simudzakhala nao mtima wina; koma iye wakubvuta inu, angakhale ali yani, adzasenza citsutso cace.

11. Koma ine, abale, ngati ndilalikiransoindulidwe, ndizunzikanso bwanji? Pamenepo cikhumudwitso ca mtanda cidatha.

12. Mwenzi atadzidula, iwo akugwedezetsani inu.

Agalatiya 5