Agalatiya 5:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Koma ine, abale, ngati ndilalikiransoindulidwe, ndizunzikanso bwanji? Pamenepo cikhumudwitso ca mtanda cidatha.

12. Mwenzi atadzidula, iwo akugwedezetsani inu.

13. Pakuti adakuitanani inu, abale, mukhale mfulu; cokhaco musacite nao ufulu wanu cothandizira thupi, komatu mwa cikondi citiranani ukapolo.

14. Pakuti mau amodzi akwaniritsa cilamulo conse ndiwo; Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.

15. Koma ngati mulumana ndi kudyana, cenjerani mungaonongane.

16. Koma ndinena, Muyendeyende ndi Mzimu, ndipo musafitse cilakolako ca thupi.

Agalatiya 5