1. Agalatiya opusa inu, anakulodzani ndani, inu amene Kristu anaonetsedwa pa maso panu, wopacikidwa?
2. ici cokha ndifuna kuphunzira kwa inu, Kodi munalandira Mzimuyo ndi nchito za lamulo, kapena ndi kumva kwa cikhulupiriro?
3. Kodi muli opusa otere? Popeza mudayamba ndi Mzimu, kodi tsopano mutsiriza ndi thupi?