Agalatiya 1:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. kapena kukwera kunka ku Yerusalemu sindinankako kwa iwo amene anakhala atumwi ndisanakhale mtumwi ine, komatu ndinamuka ku Arabiya, ndipo ndinabweranso ku Damasiko.

18. Pamenepo patapita zaka zitatu, ndinakwera kunka ku Yerusalemu kukazindikirana naye Kefa, ndipo ndinakhala kwa iye masiku khumi ndi asanu.

19. Koma wina wa atumwi sindinamuona, koma Yakobo mbale wa Ambuye.

20. Ndipo izi ndikulemberani inu, taonani, pamaso pa Mulungu sindinama ine.

Agalatiya 1