4. munthu yense asapenyerere zace za iye yekha, koma yense apenyererenso za mnzaceo
5. Mukhale nao mtima m'kati mwanu umene unalinso mwa Kristu Yesu,
6. ameneyo, pokhala nao maonekedwe a Mulungu, sanaciyesa colanda kukhala wofana ndi Mulungu,
7. koma anadzikhuthula yekha, natenga maonekedwe akapolo, nakhala m'mafanizidwe a anthu;
8. ndipo popezedwa m'maonekedwe ngati munthu, anadzicepetsa yekha, nakhala womvera kufikira imfa, ndiyo imfa ya pamtanda.