Afilipi 1:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. ndi kuti unyinji wa abale mwa Ambuye, pokhulupirira m'zomangira zanga, alimbika mtima koposa kulankhula mau a Mulungu opanda mantha.

15. Enatu alalikiranso Kristu cifukwa ca kaduka ndi ndeu; koma enanso cifukwa ca kukoma mtima;

16. ena atero ndi cikondi, podziwa kuti anandiika ndicite eokanira ca Uthenga Wabwino;

17. koma ena alalikira Kristu mocokera m'cotetana, kosati koona, akuyesa kuti adzandibukitsira cisautso m'zomangira zanga.

18. Potero nciani? Cokhaco kuti monsemo, ngati pamaso pokha, ngati m'coonadi, Kristu alalikidwa; ndipo m'menemo ndikondwera, komanso ndidzakondwera.

19. Pakuti ndidziwa kuti ici cidzandicitira ine cipulumutso, mwa pembedzero lanu ndi mwa kundipatsako kwa Mzimu wa Yesu Kristu;

Afilipi 1