Aefeso 6:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Koma 2 kuti mukadziwe inunso za kwa ine, zimene ndicita, zinthu zonse adzakuzindikiritsani Tukiko mbale wokondedwayo, ndi mtumiki wokhulupirika mwa Ambuye;

22. amene ndamtuma kwa inu cifukwa ca icico, kuti mukazindikire za kwa ife, ndi kuti akatonthoze mitima yanu.

23. 3 Mtendere ukhale kwa abale, ndi cikondi, pamodzi ndi cikhulupiriro, zocokera kwa Mulungu Atate, ndi Ambuye Yesu Kristu.

24. Akhale naco cisomo onse akukonda Ambuye wathu Yesu Kristu m'eosaonongeka.

Aefeso 6