Aefeso 4:5-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ambuye mmodzi, cikhulupiriro cimodzi, ubatizo umodzi,

6. Mulungu mmodzi ndi Atate wa onse amene ali pamwamba pa onse, ndi mwa onse, ndi m'kati mwa zonse.

7. Ndipo kwa yense wa ife capatsika cisomo, monga mwa muyeso wa mphatso ya Kristu.

8. Cifukwa cace anena,M'mene anakwera kumwamba, anamanga ndende undende,Naninkha zaufulu kwa anthu.

9. Koma ici, cakuti, Anakwera, nciani nanga komakuti anatsikiranso ku madera a kunsi kwa dziko?

10. Iye wotsikayo ndiye yemweyonso anakwera, popitiriratu miyamba yonse, kuti akadzaze zinthu zonse.

11. Ndipo Iye anapatsa ena akhale atumwi; ndi enaaneneri; ndi ena alaliki; ndi ena abusa, ndi ena aphunzitsi;

12. kuti akonzere oyera mtima: ku nchito ya utumiki, kumangirira thupi la Kristu;

13. kufikira ife tonse tikafikira ku umodzi wa cikhulupiriro, ndi wa cizindikiritso ca Mwana wa Mulungu, kwa munthu wangwiro, ku muyeso wa msinkhu wa cidzaloca Kristu.

Aefeso 4