Aefeso 4:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. ndi kusamalitsa kusunga umodzi wa Mzimu mwa cimangiriro ca mtendere.

4. Thupi limodzi ndi Mzimu mmodzi, monganso anakuitanani m'ciyembekezo cimodzi ca maitanidwe anu;

5. Ambuye mmodzi, cikhulupiriro cimodzi, ubatizo umodzi,

6. Mulungu mmodzi ndi Atate wa onse amene ali pamwamba pa onse, ndi mwa onse, ndi m'kati mwa zonse.

7. Ndipo kwa yense wa ife capatsika cisomo, monga mwa muyeso wa mphatso ya Kristu.

8. Cifukwa cace anena,M'mene anakwera kumwamba, anamanga ndende undende,Naninkha zaufulu kwa anthu.

Aefeso 4