Aefeso 4:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Pamenepo ndinena ici, ndipo ndicita umboni mwa Ambuye, kuti simuyendanso inu monganso amitundu angoyenda, m'citsiru ca mtima wao,

18. odetsedwam'nzeru zao, oyesedwa alendo pa moyo wa Mulungu, cifukwa ca cipulukiro ciri mwa iwo, cifukwa ca kuumitsa kwa mitima yao;

19. amenewo popeza sazindikiranso kanthu konse, anadzipereka okha kuti akhumbe zonyansa, kuti acite cidetso conse mu umbombo.

20. Koma inusimunaphunzira Kristu cotero,

Aefeso 4