Aefeso 4:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. koma ndi kucita zoona mwa cikondi tikakule m'zinthu zonse, kufikira iye amene ali mutu ndiye Kristu;

16. kucokera mwa Iye thupi lonse, lokowanidwa ndi lolumikizidwa pamodzi, pothandizanapo mfundo yonse, monga mwa kucititsa kwa ciwalo conse pa muyeso wace, licita makulidwe a thupi, kufikira cimango cace mwa cikondi.

17. Pamenepo ndinena ici, ndipo ndicita umboni mwa Ambuye, kuti simuyendanso inu monganso amitundu angoyenda, m'citsiru ca mtima wao,

18. odetsedwam'nzeru zao, oyesedwa alendo pa moyo wa Mulungu, cifukwa ca cipulukiro ciri mwa iwo, cifukwa ca kuumitsa kwa mitima yao;

Aefeso 4