Aefeso 3:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Cifukwa ca ici ine Paulo, ndine wandende wa Kristu Yesu cifukwa ca inu amitundu,

2. ngatitu munamva za udindo wa cisomo ca Mulungucimene anandipatsa ine ca kwa inu;

3. ndi umo anandizindikiritsa cinsinsico mwa bvumbulutso, monga ndinalemba kale mwacidule,

4. cimene mukhoza kuzindikira naco, pakuciwerenga, cidziwitso canga m'cinsinsi ca Kristu,

5. cimene sanacizindikiritsa ana a anthu m'mibadwo yina, monga anacibvumbulutsa tsopano kwa atumwi ndi aneneri ace oyera mwa Mzimu,

Aefeso 3